Soundtracks: A B C D E F G H I J K L M N O P Q R S T U V W X Y Z #

List of artists: A B C D E F G H I J K L M N O P Q R S T U V W X Y Z #


Malawi Native Anthem Text


Nation Of 1 Lyrics

 

Malawi Native Anthem Text Lyrics

Malawi Native Anthem Text by Nation Of 1


1.
Mlungu dalitsani Malawi,
Mumsunge m'mtendere.
Gonjetsani adani onse,
Njala, nthenda, nsanje.
Lunzitsani mitima yathu,
Kuti tisaope.
Mdalitse Mtsogo leri na fe,
Ndi Mai Malawi.
2.
Malawi ndziko lokongola,
La chonde ndi ufulu,
Nyanja ndi mphepo ya m'mapiri,
Ndithudi tadala.
Zigwa, mapiri, nthaka, dzinthu,
N'mphatso zaulere.
Nkhalango, madambo abwino.
Ngwokoma Malawi.
3.
O! Ufulu tigwirizane,
Kukweza Malawi.
Ndi chikondi, khama, kumvera,
Timutumikire.
Pa nkhondo nkana pa mtendere,
Cholinga n'chimodzi.
Mai, bambo, tidzipereke,
Pokweza Malawi.
Sent by Carlos André Pereira da Silva Branco



A-Z Lyrics Universe

Lyrics / song texts are property and copyright of their owners and provided for educational purposes.