Malawi Native Anthem Text Lyrics
by Unknown
Buy album CD:
Other Songs HE - PAN
1.
Mlungu dalitsani Malawi,
Mumsunge m'mtendere.
Gonjetsani adani onse,
Njala, nthenda, nsanje.
Lunzitsani mitima yathu,
Kuti tisaope.
Mdalitse Mtsogo leri na fe,
Ndi Mai Malawi.
2.
Malawi ndziko lokongola,
La chonde ndi ufulu,
Nyanja ndi mphepo ya m'mapiri,
Ndithudi tadala.
Zigwa, mapiri, nthaka, dzinthu,
N'mphatso zaulere.
Nkhalango, madambo abwino.
Ngwokoma Malawi.
3.
O! Ufulu tigwirizane,
Kukweza Malawi.
Ndi chikondi, khama, kumvera,
Timutumikire.
Pa nkhondo nkana pa mtendere,
Cholinga n'chimodzi.
Mai, bambo, tidzipereke,
Pokweza Malawi.
Sent by Carlos André Pereira da Silva Branco
|
|
Unknown - Malawi Native Anthem Text song words/lyrics from Other Songs HE - PAN album cd are property
& copyright of their owners and provided for educational purposes for free. Visit Unknown Lyrics page to find new songs. |
|